Salimo 51:1-19

  • Pemphero la munthu wolapa

    • Wochimwa kuchokera pamene mayi anatenga pakati (5)

    • ‘Ndiyeretseni ku machimo anga’ (7)

    • “Lengani mtima wolungama mkati mwanga” (10)

    • Mulungu amasangalala ndi kudzimvera chisoni mumtima (17)

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide, pa nthawi imene mneneri Natani anapita kwa iye, Davideyo atagona ndi Bati-seba.+ 51  Ndikomereni mtima inu Mulungu, mogwirizana ndi chikondi chanu chokhulupirika.+ Fufutani zolakwa zanga mogwirizana ndi chifundo chanu chachikulu.+   Mundisambitse bwinobwino nʼkuchotsa cholakwa changa,+Ndiyeretseni ku tchimo langa.+   Chifukwa zolakwa zanga ndikuzidziwa bwino,Ndipo tchimo langa lili pamaso panga* nthawi zonse.+   Inuyo ndi amene ndakuchimwirani kwambiri kuposa aliyense.*+Ndachita chinthu chimene mumachiona kuti ndi choipa.+ Choncho mukamalankhula, mumalankhula zachilungamo,Ndipo mukamaweruza, mumaweruza mwachilungamo.+   Taonani! Ndinabadwa ndili wochimwa,Ndipo ndine wochimwa kuchokera pamene mayi anga anatenga pakati panga.+   Taonani! Mumasangalala ndi choonadi chochokera pansi pa mtima.+Ndiphunzitseni* kuti ndikhale ndi mtima wanzeru.   Ndiyeretseni ndi hisope* ku machimo anga kuti ndikhale woyera.+Ndisambitseni kuti ndiyere kwambiri kuposa matalala.+   Ndichititseni kumva kufuula kokondwera ndi kosangalala,Kuti ndisangalale ngakhale kuti mwathyola mafupa anga.+   Ndikhululukireni* machimo anga,+Ndipo fufutani* zolakwa zanga zonse.+ 10  Inu Mulungu, lengani mtima wolungama mkati mwanga,+Ndipo sinthani mmene ndimaganizira+ kuti ndikhale wokhulupirika. 11  Musandichotse pamaso panu nʼkunditaya.Ndipo musandichotsere mzimu wanu woyera. 12  Bwezeretsani mwa ine chisangalalo chimene chimabwera chifukwa cha chipulumutso chanu.+Ndipatseni mtima wofunitsitsa kukumverani.* 13  Anthu olakwa ndidzawaphunzitsa njira zanu,+Kuti ochimwawo abwerere kwa inu. 14  Inu Mulungu, ndipulumutseni ku mlandu wa magazi,+ inu Mulungu wa chipulumutso changa,+Kuti lilime langa lilengeze mosangalala kuti ndinu wolungama.+ 15  Inu Yehova, tsegulani milomo yangayi,Kuti pakamwa panga patamande inu.+ 16  Chifukwa nsembe simukuifuna, mukanakhala kuti mukuifuna ndikanaipereka kwa inu.+Inu simusangalala ndi nsembe yopsereza yathunthu.+ 17  Nsembe zimene Mulungu amasangalala nazo ndi kudzimvera chisoni mumtima.Inu Mulungu, simudzakana* mtima wosweka ndi wophwanyika.+ 18  Chitirani Ziyoni zabwino mwa kukoma mtima kwanu.Ndipo mangani mpanda wa Yerusalemu. 19  Mukatero mudzasangalala ndi nsembe zachilungamo,Mudzakondwera ndi nsembe zopsereza komanso nsembe zathunthu.Pamenepo ngʼombe zamphongo zidzaperekedwa paguwa lanu la nsembe.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “mʼmaganizo mwanga.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Inu nokha.”
Kapena kuti, “Phunzitsani umunthu wanga wamkati.”
Kapena kuti, “Bisani nkhope yanu kuti isaone.”
Kapena kuti, “fafanizani.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndichirikizeni ndi mzimu wofunitsitsa.”
Kapena kuti, “simudzanyoza.”