Pitani ku nkhani yake

Zimene Baibulo Limaphunzitsa

Baibulo limatithandiza kupeza mayankho a mafunso ovuta kwambiri amene tingafunse pa moyo wathu. Ndipo kwa zaka zambirimbiri, mfundo zimene zili m’Baibulo zakhala zikuthandiza anthu kwambiri. M’chigawo chino, mupeza mfundo zotsimikizira kuti Baibulo ndi lothandizadi.—2 Timoteyo 3:16, 17.

Zina Zimene Zilipo

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi Maulosi Onena za Mesiya Amatsimikizira Kuti Yesu Analidi Mesiya?

Kodi a Mesiya analipo angapo?

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi Maulosi Onena za Mesiya Amatsimikizira Kuti Yesu Analidi Mesiya?

Kodi a Mesiya analipo angapo?

Kuphunzira Baibulo ndi Mboni za Yehova

Yambani kuphunzira Baibulo

Phunzirani Baibulo kwaulere, mochita kukambirana ndi mphunzitsi wanu.

Pemphani Kuti Tidzakuyendereni

Mutha kukhala ndi mwayi wokambirana nkhani inayake ya m’Baibulo kapena kudziwa zambiri zokhudza Mboni za Yehova.

Zokuthandizani Pophunzira Baibulo

Sankhani zinthu zokuthandizani pophunzira Baibulo zimene zingapangitse kuphunzira kukhala kopindulitsa komanso kosangalatsa.

Kodi Baibulo Lingakuthandizeni Bwanji?

Mtendere Komanso Moyo Wosangalala

Baibulo lathandiza anthu ambirimbiri kupirira mavuto, kuchepetsako nkhawa komanso kuthana ndi mavuto ena ndipo lawathandizanso kuona kuti moyo uli ndi cholinga.

Kukhulupirira Mulungu

Chikhulupiriro n’champhamvu kwambiri ndipo chimathandiza munthu kukhala ndi mtendere wam’maganizo panopa komanso chiyembekezo chodalirika cham’tsogolo.

Anthu Okwatirana Komanso Mabanja

Anthu okwatirana komanso mabanja amakumana ndi mavuto ambiri. Koma malangizo amene amachokera m’Baibulo angathandize kuti anthu a m’banja azigwirizana komanso azisangalala.

Malangizo Othandiza Achinyamata

Werengani nkhanizi kuti mudziwe mmene Baibulo lingathandizire achinyamata pa mavuto amene amakumana nawo kawirikawiri.

Zoti Ana Achite

Gwiritsani ntchito zinthu zosangalatsa zimenezi, nkhani zochokera m’Baibulo komanso makadi a anthu otchulidwa m’Baibulo pophunzitsa ana mfundo za m’Baibulo.

Kodi Baibulo Limanena Zotani?

Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Werengani kuti mudziwe mayankho a m’Baibulo a mafunso osiyanasiyana okhudza Mulungu, Yesu, banja, mavuto ndi zinthu zina zambiri.

Kufotokoza Mavesi a M’Baibulo

Dziwani tanthauzo lenileni la mavesi komanso mawu ena odziwika bwino a m’Baibulo.

Mbiri Komanso Baibulo

Werengani kuti mudziwe zimene zinachitika kuti Baibulo lifikebe mpaka nthawi yathu. Fufuzani umboni wosonyeza kuti ndi lolondola komanso lodalirika.

Baibulo Komanso Sayansi

Kodi Baibulo limagwirizana ndi zimene asayansi amaphunzitsa? Kuyerekezera zimene Baibulo limanena ndi zimene asayansi apeza kungatithandize kupeza yankho la funsoli.