Wolembedwa ndi Yohane 14:1-31

  • Yesu ndi njira yokhayo yotifikitsa kwa Atate (1-14)

    • “Ine ndine njira, choonadi ndi moyo” (6)

  • Yesu analonjeza mzimu woyera (15-31)

    • ‘Atate ndi wamkulu kuposa ine’ (28)

14  “Mitima yanu isavutike.+ Khulupirirani Mulungu,+ khulupiriraninso ine.  Mʼnyumba ya Atate wanga muli malo ambiri okhalamo. Mukanakhala kuti mulibe malo ndikanakuuzani, chifukwa ndikupita kukakukonzerani malo.+  Ndiye ndikapita kukakukonzerani malowo, ndidzabweranso kudzakutengerani kwathu, kuti kumene ine ndikakhale inunso mukakhale komweko.+  Ndipo kumene ine ndikupita, njira yake mukuidziwa.”  Tomasi+ anafunsa kuti: “Ambuye, ife sitikudziwa kumene mukupita. Ndiye njira yake tingaidziwe bwanji?”  Yesu anamuuza kuti: “Ine ndine njira,+ choonadi+ ndi moyo.+ Palibe amene amafika kwa Atate osadzera mwa ine.+  Anthu inu mukanakhala kuti mukundidziwa, mukanadziwanso Atate wanga. Kuyambira panopa muwadziwa ndipotu mwawaona kale.”+  Filipo anamuuza kuti: “Ambuye, tionetseni Atatewo ndipo tikhutira.”  Yesu anamuuza kuti: “Kodi iwe Filipo sukundidziwabe ngakhale kuti anthu inu ndakhala nanu nthawi yayitali yonseyi? Amene waona ine waonanso Atate.+ Nanga iwe bwanji ukunena kuti, ‘Tionetseni Atateʼ? 10  Kodi sukukhulupirira kuti Atate ndi ine ndife ogwirizana?+ Zinthu zimene ndimakuuzani sindilankhula zamʼmaganizo mwanga,+ koma Atate amene ndi wogwirizana ndi ine ndi amene akuchita ntchito zake kudzera mwa ine. 11  Khulupirira zimene ndanena kuti ine ndi Atate ndife ogwirizana, apo ayi, ingokhulupirira chifukwa cha ntchito zokhazi.+ 12  Ndithudi ndikukuuzani, aliyense wokhulupirira ine, nayenso adzachita ntchito zimene ine ndimachita, ndipo adzachita ntchito zazikulu kuposa zimenezi+ chifukwa ine ndikupita kwa Atate.+ 13  Komanso chilichonse chimene mudzapemphe mʼdzina langa, ine ndidzachichita, kuti Atate alemekezedwe kudzera mwa Mwana wake.+ 14  Ngati mutapempha chilichonse mʼdzina langa, ine ndidzachichita. 15  Ngati mumandikonda, mudzasunga malamulo anga.+ 16  Ine ndidzapempha Atate ndipo adzakupatsani mthandizi* wina kuti adzakhale nanu mpaka kalekale.+ 17  Mthandizi ameneyo ndi mzimu wa choonadi+ umene dziko silingaulandire, chifukwa siliuona kapena kuudziwa.+ Inu mumaudziwa chifukwa umakhala mwa inu ndipo uli mwa inu. 18  Sindikusiyani ngati ana amasiye. Ndidzabwera kwa inu.+ 19  Kwatsala kanthawi kochepa ndipo dziko silidzandionanso. Koma inu mudzandiona,+ chifukwa ndili ndi moyo ndipo inunso mudzakhala ndi moyo. 20  Pa tsiku limenelo mudzadziwa kuti ine ndi wogwirizana ndi Atate komanso inu ndi ine ndife ogwirizana.+ 21  Aliyense amene ali ndi malamulo anga ndipo amawatsatira, ndi amene amandikonda. Komanso amene amandikonda, Atate wanga adzamukondanso. Inenso ndidzamukonda ndipo ndidzadzionetsera bwinobwino kwa iye.” 22  Yudasi+ wina, osati Isikariyoti, anamufunsa kuti: “Ambuye, nʼchifukwa chiyani mukufuna kudzionetsera bwinobwino kwa ife koma osati kudzikoli?” 23  Yesu anamuyankha kuti: “Ngati munthu amandikonda, adzasunga mawu anga+ ndipo Atate wanga adzamukonda komanso tidzapita kwa iwo nʼkukakhala nawo.+ 24  Amene samandikonda sasunga mawu anga, ndipo mawu amene mukumvawa si anga, koma ndi a Atate amene anandituma.+ 25  Ndakuuzani zimenezi pamene ndidakali ndi inu. 26  Koma mthandizi, amene ndi mzimu woyera umene Atate wanga adzatumize mʼdzina langa, adzakuphunzitsani komanso kukukumbutsani zinthu zonse zimene ndinakuuzani.+ 27  Ndikukusiyirani mtendere ndipo ndikupatsani mtendere wanga.+ Sindikuupereka kwa inu ngati mmene dziko limauperekera. Mitima yanu isavutike kapena kuchita mantha. 28  Mwamva ndikukuuzani kuti, ‘Ndikupita ndipo ndidzabweranso kwa inu.’ Ngati mumandikonda, mukanasangalala kuti ndikupita kwa Atate wanga, chifukwa Atate ndi wamkulu kuposa ine.+ 29  Choncho ndakuuzani zisanachitike, kuti zikachitika mukhulupirire.+ 30  Sindilankhula nanu zambiri chifukwa wolamulira wa dziko+ akubwera ndipo alibe mphamvu pa ine.+ 31  Koma kuti dziko lidziwe kuti ndimakonda Atate, ndikuchita zinthu mogwirizana ndi zimene Atatewo anandilamula.+ Nyamukani, tiyeni tichokeko kuno.”

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “adzakupatsani wolimbikitsa.”