Phunzitsani Ana Anu

Makolo, gwiritsani ntchito nkhanizi pophunzitsa ana anu mfundo zofunika kwambiri za m’Baibulo.

Mawu Oyamba

Mawu a m’buku la Deuteronomo angakuthandizeni polera ana.

PHUNZIRO

Chinsinsi Chimene Tonsefe Timafuna Titachidziwa

Baibulo limanena kuti pali nkhani inayake yachinsinsi ndipo limati nkhani imeneyi ndi “chinsinsi chopatulika.” Kodi ukufuna kudziwa chinsinsi chimenechi?

PHUNZIRO

Rabeka Ankafuna Kusangalatsa Yehova

Kodi tingatani kuti tifanane ndi Rabeka? Werengani nkhaniyi kuti mudziwe zambiri.

PHUNZIRO

Rahabi Ankakhulupirira Yehova

Werengani nkhaniyi kuti mmene Rahabi ndi abale ake anapulumukira pamene mzinda wa Yeriko unkawonongedwa.

PHUNZIRO

Anasangalatsa Bambo Ake Komanso Yehova

Kodi mwana wa Yefita ana anakwaniritsa lonjezo liti? Kodi tingatani kuti titsatire chitsanzo chake?

PHUNZIRO

Samueli Anapitiriza Kuchita Zinthu Zabwino

Kodi mungatsanzire bwanji chitsanzo cha Samueli?

PHUNZIRO

Davide Sankachita Mantha

Werengani nkhaniyi m’Baibulo kuti mudziwe zimene zinamuthandiza Davide kuti akhale wolimba mtima.

PHUNZIRO

Kodi Nthawi Zina Umaona Kuti Uli Wekha?

Kodi Yehova anauza chiyani Eliya atayamba kumva ngati kuti watsala yekha? Kodi mukuphunzirapo chiyani pa zimene zinachitikira Eliya?

PHUNZIRO

Yosiya Anali ndi Anzake Abwino

Baibulo limatiuza kuti zinali zovuta kwambiri kwa mnyamata wina, dzina lake Yosiya, kuti achite zinthu zabwino. Werengani nkhaniyi kuti mudziwe mmene anzake a Yosiya anamuthandizira kuti azichita zinthu zabwino.

PHUNZIRO

Yeremiya Sanasiye Kulankhula za Yehova

Ngakhale kuti anthu ankaseka Yeremiya komanso kumukwiyira, n’chifukwa chiyani anapitirizabe kulankhula za Mulungu?

PHUNZIRO

Yesu Anali Womvera

Nthawi zina kumvera n’kovuta. Werengani nkhaniyi kuti muone mmene chitsanzo cha Yesu chingakuthandizireni.

PHUNZIRO

Analemba za Yesu

Werengani nkhaniyi kuti mudziwe za anthu 8 omwe analemba Baibulo omwe anakhala ndi moyo m’nthawi imenenso Yesu anali padziko lapansi ndipo analemba za moyo wa Yesuyo.

PHUNZIRO

Mwana wa Mchemwali wake wa Paulo Anali Wolimba Mtima

Zimene anachitazo zinapulumutsa moyo wa ankolo ake. Kodi mukudziwa zimene anachita?

PHUNZIRO

Timoteyo Ankafuna Kuthandiza Anthu

Kodi iweyo ungatani kuti ukhale ndi moyo wosangalala ngati Timoteyo?

PHUNZIRO

Ufumu Umene Udzalamulira Dziko Lonse

Kodi zinthu zidzakhala bwanji Yesu akadzayamba kulamulira dziko lapansi? Kodi mukufuna kudzaona zimene zidzachitike pa nthawi imeneyo?