Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 110

“Chimwemwe Chimene Yehova Amapereka”

“Chimwemwe Chimene Yehova Amapereka”

(Nehemiya 8:10)

  1. 1. Zizindikiro zasonyeza kuti

    Ufumu wayandikira.

    Chipulumutso chayandikiradi.

    Tukulani mitu yanu.

    (KOLASI)

    Chimwemwe chochoka kwa Yehova

    Ndi malo achitetezo.

    Imbani mofuula ndi chimwemwe

    Chifukwa cha chiyembekezo.

    Chimwemwe chochoka kwa Yehova

    Ndi malo achitetezo.

    Tilambire M’lungu modzipereka.

    Tim’tumikire mwachimwemwe.

  2. 2. Inu nonse okondadi Yehova

    Muzimukhulupirira.

    Imirirani ndipo fuulani.

    Imbani mosangalala.

    (KOLASI)

    Chimwemwe chochoka kwa Yehova

    Ndi malo achitetezo.

    Imbani mofuula ndi chimwemwe

    Chifukwa cha chiyembekezo.

    Chimwemwe chochoka kwa Yehova

    Ndi malo achitetezo.

    Tilambire M’lungu modzipereka.

    Tim’tumikire mwachimwemwe.