NYIMBO 133
Lambirani Yehova Mudakali Achinyamata
-
1. Anyamata ndi atsikanafe
Ndife ofunika kwa Mulungu.
Tikamam’tumikira mwakhama
Azitidalitsa nthawi zonse.
-
2. Timasonyeza chikondi chathu
Tikamalemekeza makolo.
Anthu ndi M’lungu amatikonda
Ndipo timayandikira M’lungu.
-
3. Tizikumbukira M’lungu wathu.
Tikonde choonadi kwambiri.
Tikakhulupirika kwa iye
Tizisangalatsa mtima wake.
(Onaninso Sal. 71:17; Maliro 3:27; Aef. 6:1-3.)