Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 151

Iye Adzaitana

Iye Adzaitana

(Yobu 14:​13-15)

  1. 1. Moyo wathu sumachedwa kutha,

    Timafadi mwamsanga.

    Mukanthawi kochepa kwambiri

    Timayamba kulira.

    Kodi akufa angadzauke?

    M’lungu akulonjeza:

    (KOLASI)

    Iye adzawaitana,

    Akufa adzayankha.

    Akulakalakatu

    Ntchito ya manja ake.

    Mulungu adzatidzutsa

    Chonde musakaike.

    Tidzakhala kosatha

    Mongadi anthu ake.

  2. 2. Anthu a M’lungu akamwalira

    Iye sawaiwala.

    Akuwakumbukira onsewo,

    Iye adzawadzutsa

    Ndipo tonsefe tidzakhaladi

    Ndi moyo mpaka kale.

    (KOLASI)

    Iye adzawaitana,

    Akufa adzayankha.

    Akulakalakatu

    Ntchito ya manja ake.

    Mulungu adzatidzutsa

    Chonde musakaike.

    Tidzakhala kosatha

    Mongadi anthu ake.