Pitani ku nkhani yake

DECEMBER 2, 2020
NKHANI ZA PADZIKO LONSE

Mphepo Yamkuntho Yotchedwa Iota Yasakaza ku Colombia Komanso ku Central America ndi ku Mexico

Mphepo Yamkuntho Yotchedwa Iota Yasakaza ku Colombia Komanso ku Central America ndi ku Mexico

Malo

Central America, Colombia ndi Mexico

Ngozi yake

  • Pa 15 ndi 16 November 2020, mphepo yamkuntho yotchedwa Iota yomwe inali yamphamvu kwambiri inawononga m’madera akumpoto kwa Colombia, makamaka m’zilumba za San Andrés ndi Providencia ku Nyanja Yaikulu ya Caribbean

  • Mphepoyi inachititsa kuti kugwe chimvula champhamvu komanso nthaka inagumuka

  • Pa 16 November 2020, mphepo yamkuntho ya Iota inawomba ku Nicaragua kenako inafikanso m’madera ena a ku Central America. Mphepoyi inachititsa kuti zinthu zambiri ziwonongeke chifukwa chakumayambiriro kwa mweziwu, m’maderawa munawombanso mphepo ina yamkuntho yotchedwa Eta

Mmene ngoziyi yakhudzira abale ndi alongo athu

Central America

  • Costa Rica

    • Ofalitsa 22 anafunika kuchoka m’nyumba zawo

  • Guatemala

    • Ofalitsa 93 anafunika kuchoka m’nyumba zawo

  • Honduras

    • Ofalitsa 1,531 anafunika kuchoka m’nyumba zawo

    • Ofalitsa awiri anavulala pang’ono

  • Nicaragua

    • Ofalitsa 75 anafunika kuchoka m’nyumba zawo

  • Panama

    • Ofalitsa 16 anafunika kuchoka m’nyumba zawo

Colombia

    • Wofalitsa mmodzi wa ku Providencia anathyoka mkono

    • Wofalitsa mmodzi wa ku San Andrés anavulala pang’ono

Mexico

    • Ofalitsa 1,248 anachoka m’nyumba zawo m’madera a Tabasco ndi Veracruz

Katundu yemwe wawonongeka

Central America

  • Costa Rica

    • Nyumba 9 zinawonongeka

  • Guatemala

    • Nyumba 18 zinawonongeka

    • Nyumba za Ufumu 7 zinawonongeka pang’ono

    • Nyumba za Ufumu ziwiri zinawonongeka kwambiri

  • Honduras

    • Nyumba za Ufumu 7 zinawonongeka pang’ono

    • Nyumba 227 zinawonongeka

  • Nicaragua

    • Nyumba 106 zinawonongeka

    • Nyumba za Ufumu zitatu zinawonongeka pang’ono

  • Panama

    • Nyumba 5 zinawonongeka

    • Nyumba za Ufumu ziwiri zinawonongeka kwambiri

Colombia

    • Malipoti oyambirira akusonyeza kuti nyumba za abale zambiri zinawonongeka kwambiri ku Providencia komanso Nyumba ya Ufumu imodzi inagweratu. Panopa zikumavuta kulumikizana ndi abale ndi alongo omwe amakhala pazilumbazi chifukwa choti mawaya a magetsi ndi a telefoni anaduka

    • Nyumba 20 komanso Nyumba ya Ufumu imodzi ku San Andrés zinawonongeka pang’ono

Mexico

    • Nyumba 184 zinawonongeka

Nyumba ya Ufumu ya ku Providencia, Colombia, mphepo yamkuntho ya Iota isanawombe komanso pambuyo pake

Ntchito yothandiza anthu

  • Komiti ya Nthambi ku Colombia yakhazikitsa Komiti Yothandiza pa Ngozi Zogwa Mwadzidzidzi kuti igwire ntchito yothandiza ofalitsa. Komitiyi ikugwira ntchito limodzi ndi woyang’anira dera m’chigawochi popereka zinthu zofunika komanso kulimbikitsa abale ndi alongo ndi mfundo za m’Baibulo

  • Ofesi ya Nthambi ya Central America inakhazikitsa makomiti 4 othandiza pa ngozi zogwa mwadzidzidzi kuti athandize abale ndi alongo omwe anakhudzidwa ndi mphepo ya Eta ndiponso ya lota ku Central America ndi ku Mexico. Oyang’anira madera akulimbikitsa komanso kupereka zinthu zofunika ku mabanja okhudzidwa. Komanso, mipingo ya kumeneko yapereka maphukusi oposa 400 a chakudya kuti chithandize abale ndi alongo a ku Honduras ndi ku Nicaragua. Abale ndi alongo ena omwe anachoka m’nyumba zawo akukhala m’nyumba za a Mboni amene ali m’madera omwe sanakhudzidwe ndi mphepozi

  • Abale ndi alongo omwe akugwira nawo ntchito yothandiza anthu okhudzidwa akuyesetsa kutsatira malangizo opewera mliri wa COVID-19 n’cholinga choti akhale otetezeka pogwira ntchitoyi

Ngakhale kuti sizingatheke kuti abale ndi alongo athuwa apeweretu kukumana ndi mavuto osiyanasiyana m’dzikoli kuphatikizapo omwe amabwera chifukwa cha ngozi zam’chilengedwe, iwo sakukayikira kuti Yehova Mulungu wathu awathandiza ndipo akhala malo awo achitetezo.—Salimo 142:5.