Pitani ku nkhani yake

Kodi Ndingatchule Zinthu Ziti Popemphera?

Kodi Ndingatchule Zinthu Ziti Popemphera?

Yankho la m’Baibulo

 Popemphera mukhoza kutchula chinthu chilichonse chogwirizana ndi zimene Mulungu amafuna. Pa mfundo imeneyi, Baibulo limati: “Chilichonse chimene tingamupemphe [Mulungu] mogwirizana ndi chifuniro chake, amatimvera.” (1 Yohane 5:14) Kodi muyenera kutchulanso mavuto anu? Inde. Baibulo limati: “Mukhuthulireni [Mulungu] za mumtima mwanu.”—Salimo 62:8.

Zinthu zimene tingapemphe

  •   Kuti tizikhulupirira kwambiri Mulungu.—Luka 17:5.

  •   Kuti mzimu woyera, kapena kuti mphamvu imene Mulungu amagwiritsa ntchito, uzitithandiza kuchita zabwino.—Luka 11:13.

  •   Kuti atipatse mphamvu zoti tithe kulimbana ndi mavuto athu komanso tipirire mayesero.—Afilipi 4:13.

  •   Kuti atipatse mtendere wamumtima.—Afilipi 4:6, 7.

  •   Kuti atipatse nzeru zotithandiza kuti tizitha kusankha bwino zochita.—Yakobo 1:5.

  •   Kuti atipatse zinthu zofunikira pa moyo wa tsiku ndi tsiku.—Mateyu 6:11.

  •   Kuti atikhululukire machimo athu.—Mateyu 6:12.