NYIMBO 69
Patsogolo na Ulaliki wa Ufumu!
(2 Timoteyo 4:5)
-
1. Pitani, kalalikileni
Kwa amitundu yonse.
Na mtima wokonda anansi,
Thandizani ofatsa.
Ni mwayi wathu kulengeza
Za Ufumu wa Yehova.
Mokondwa tiphunzitsa ena,
Za dzina lake loyela.
(KOLASI)
Lalikani uthenga wa Ufumu
konse konse.
Khalanibe okhulupilika
kwa M’lungu wathu.
-
2. Capamodzi titumikile
Yehova, ‘tate wathu.
Odzozedwa na nkhosa zina,
Tiphunzitse co’nadi.
Onse tiŵauze uthenga,
Wa Ufumu wa Yehova.
Tilengeza molimba mtima
Timadalila Yehova.
(KOLASI)
Lalikani uthenga wa Ufumu
konse konse.
Khalanibe okhulupilika
kwa M’lungu wathu.
(Onaninso Sal. 23:4; Mac. 4:29, 31; 1 Pet. 2:21.)