Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 135

Yehova Akutipempha Kuti: “Mwana Wanga Khala Wanzeru”

Yehova Akutipempha Kuti: “Mwana Wanga Khala Wanzeru”

(Miyambo 27:11)

  1. 1. Mwana wanga undipatse

    Mtima wako.

    Yemwe akunditonza

    Aone yekha

    Ukudziperekadi

    Mofunitsitsa.

    Anthu adziwe

    Kuti umandikonda.

    (KOLASI)

    Mwana wanga wokondedwawe

    Ukhale wanzeru chonde

    Kuti uzinditumikira,

    Inde mwakufuna kwako.

  2. 2. Uzinditumikira

    Mosangalala.

    Ngakhale ukapunthwa

    Ndidzakudzutsa.

    Ndipo ngati wina

    wakukhumudwitsa,

    Usadere nkhawa

    Ndidzakhala nawe.

    (KOLASI)

    Mwana wanga wokondedwawe

    Ukhale wanzeru chonde

    Kuti uzinditumikira,

    Inde mwakufuna kwako.