NYIMBO 136
Yehova “Akulipire Mokwanira”
-
1. Yehova amadziwa anthu onse
Omwe amam’tumikira.
Amadziwa bwino mavuto awo
Ndi zomwe amadzimana.
Ngati mwasiya abale ndi nyumba,
M’lungu akudziwa zonse.
Watipatsa abale ndi alongo,
Adzatipatsanso moyo.
(KOLASI)
Yehova akupatseni mphoto.
Akulipireni mokwanira.
Mubisale m’mapiko ake.
Ndi M’lungu woona, iye sanama.
-
2. Nthawi zina timakhala ndi nkhawa
Poganizira moyowu.
Mwinanso kupeza zofunikira
Kungamakhale kovuta.
M’lungu akudziwa zofunikazo,
Amamvanso mapemphero.
Mawu, mzimu wake ndi anzathunso
Angamatilimbikitse.
(KOLASI)
Yehova akupatseni mphoto.
Akulipireni mokwanira.
Mubisale m’mapiko ake.
Ndi M’lungu woona, iye sanama.
(Onaninso Ower. 11:38-40; Yes. 41:10.)