Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 97

Mawu a Mulungu Amatithandiza Kukhala Ndi Moyo

Mawu a Mulungu Amatithandiza Kukhala Ndi Moyo

(Mateyu 4:4)

  1. 1. Moyo umafunikira

    Mawu a Mulungu

    Kuti atitsogolere

    M’zonse timachita,

    Ndipo timasangalala

    Ndi kudalitsidwa.

    (KOLASI)

    Chakudya chofunikira

    Ndi Mawu a M’lungu.

    Moyo umafunikadi

    Mawu a Mulungu.

  2. 2. M’mawuwo timawerenga

    Za anthu akale

    Omwe anatumikira

    Mokhulupirika.

    Tikawerenga nkhanizi

    Zimalimbikitsa.

    (KOLASI)

    Chakudya chofunikira

    Ndi Mawu a M’lungu.

    Moyo umafunikadi

    Mawu a Mulungu.

  3. 3. Tikamawerenga Mawu

    Tsiku lililonse,

    Tidzathadi kupirira

    Mayesero onse.

    Ndiye tizikumbukira

    Zomwe tawerenga.

    (KOLASI)

    Chakudya chofunikira

    Ndi Mawu a M’lungu.

    Moyo umafunikadi

    Mawu a Mulungu.

(Onaninso Yos. 1:8; Aroma 15:4.)